Kuyang'anira chizindikiro cha ponsezo...
Palibe kusintha kwa ponsezo
Palibe msonkho Kwa "Query here"
Ponya ndi FlexSearch
Tsamba limene mukufuna silipo kapena linapita kumene.
“Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa…” (Aroma 6:23) Tiyeni tinene zoonadi. Zirombo zoopsya kumwa zoledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere ziri nkuopsyeza ndiponso kuononga chimene Mulungu anachilenga kukhala chokoma ndiponso chabwino. Monga mchitidwe wa Octopus wamphamvuyo, izi zimakoka ang’ono komanso aakulu ndi kuwafumbatira. Anthu ambiri amakakamizidwa pambali iliyonse ndi zokhumba zao, monga manyuzi pepala komanso ndi kuitanira kwa television. Maso ndi makutu zimalunjika kumene kuli zosokoneza zokhazokha zomwe zotsatira zake ndi kukhala ndi moyo wa uzimu komanso wa kuthupi wobwerera m’mbuyo. Temberero la chakumwa choledzeretsa, mankhwala ndi chiwerewere zaleka chitsanzo chokoma cha m’midzi yathu popanda kuongoledwa ndipo ziri nkupita ku chionongeko.
Chiyero Chikondi Kukhulupirirana Makomo osangalala Chilakolako Manyazi Mantha Makomo olekana Kusungulumwa Chiyero cha maganizo, chikumbumtima ndi thupi ndi chinthu chopindulitsa m’moyo wa munthu. Ngakhale chiyero chokha sichitanthauza umulungu, koma ndi chipatso cha chikhristu ndi dalitso kwa mtundu wa anthu. Chifukwa cha kuperewera kwa chikhalidwe chabwino amayi ndi abambo lero akulola kukhudzidwa ndi chikhalidwe chimene Buku Lopatulika limanena kuti ndi tchimo. Chikhalidwe chavomerezedwa ngati njira yabwino m’moyo uno ndi anthu ambiri. Chimene Mulungu akunena kuti tchimo, sichikhalanso ngati tchimo. Nanga zotsatira zake zidzakhala zotani?
Zimene zalembedwa m’munsi ndi zizindikiro zowonetsa moyo wa kudzikonda. Mzimu Woyera yekha ndi amene angathe kukutanthauzirani izi aliyense payekhapayekha. Pamene mukuwerenga, dziyezeni nokha pa maso penipeni pa Mulungu. ●Mzimu wobisika wa kunyada kapena wodzikuza powona mwapambana kapena mwapatsidwa udindo; chifukwa chakuti munaphunzira bwino kapenanso mawonekedwe anu; chifukwa cha nzeru kapena mphatso zanu; mzimu umene umadziwona ngati wofunika ndipo wosadalira ena? Miyambo 16:18; 20:6; 25:14; Aroma 12:3; Yakobo 4:6. ●Kukonda kuyamikidwa ndi anthu; kukonda kuti anthu awone zabwino zanu; kukonda kukhala wapamwamba, kudziwonetsera pakulankhula; kudzikuza pamene mwatha kulankhula kapena kupemphera bwino? Yohane 5:44; 12:42,43; 1 Akorinto 13:4.